Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 7:43 - Buku Lopatulika

Kudakhala tsono kusiyana m'khamulo chifukwa cha Iye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Kudakhala tsono kusiyana m'khamulo chifukwa cha Iye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Choncho khamu la anthu lidagaŵikana chifukwa cha Iye.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kotero anthu anagawikana chifukwa cha Yesu.

Onani mutuwo



Yohane 7:43
7 Mawu Ofanana  

Pakuti ndinadza kusiyanitsa munthu ndi atate wake, ndi mwana wamkazi ndi amake, ndi mkazi wokwatiwa ndi mpongozi wake:


Kodi muyesa kuti ndinadzera kudzapatsa mtendere padziko lapansi? Ndinena kwa inu, Iaitu, komatu kutsutsana;


Panakhalanso kutsutsana pakati pa Ayuda chifukwa cha mau awa.


Ndipo kunali kung'ung'udza kwambiri za Iye m'makamu a anthu; ena ananena, kuti, Ali wabwino; koma ena ananena, Iai, koma asocheretsa khamu la anthuwo.


Ena pamenepo mwa Afarisi ananena, Munthu uyu sachokera kwa Mulungu, chifukwa sasunga Sabata. Koma ena ananena, Munthu ali wochimwa akhoza bwanji kuchita zizindikiro zotere? Ndipo panali kutsutsana mwa iwo.


Ndipo khamu la mzindawo linagawikana; ena anali ndi Ayuda, koma ena anali ndi atumwi.