Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 21:4 - Buku Lopatulika

Koma pakuyamba kucha, Yesu anaimirira pambali pa nyanja, komatu ophunzirawo sanadziwe kuti ndiye Yesu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma pakuyamba kucha, Yesu anaimirira pambali pa nyanja, komatu ophunzirawo sanadziwa kuti ndiye Yesu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kutacha Yesu adaimirira pa mtunda. Komabe ophunzira aja sadazindikire kuti ndi Yesu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mmamawa, Yesu anayimirira mʼmbali mwa nyanja, koma ophunzira ake sanazindikire kuti anali Yesu.

Onani mutuwo



Yohane 21:4
5 Mawu Ofanana  

Ndipo Yosefe anazindikira abale ake, koma iwo sanamzindikire iye.


Ndipo zitatha izi, anaonekanso Iye m'maonekedwe ena kwa awiri a iwo alikuyenda kupita kumidzi.


Ndipo maso ao anatseguka, ndipo anamzindikira Iye; ndipo anawakanganukira Iye, nawachokera.


M'mene adanena izi, anacheuka m'mbuyo, naona Yesu ali chilili, ndipo sanadziwe kuti ndiye Yesu.