Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 21:10 - Buku Lopatulika

Yesu ananena nao, Tenganiko nsomba zimene mwazigwira tsopano.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yesu ananena nao, Tenganiko nsomba zimene mwazigwira tsopano.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Yesu adaŵauza kuti, “Bwera nazoni nsomba zina zimene mwapha.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesu anawawuza kuti, “Tabweretsa nsomba zina mwagwirazo.”

Onani mutuwo



Yohane 21:10
6 Mawu Ofanana  

Koma pokhala iwo chikhalire osakhulupirira chifukwa cha chimwemwe, nalikuzizwa, anati kwa iwo, Muli nako kanthu kakudya kuno?


Chifukwa chake Simoni Petro anakwera m'ngalawa nakokera khoka kumtunda lodzala ndi nsomba zazikulu, zana limodzi, ndi makumi asanu ndi zitatu; ndipo zingakhale zinachuluka kotere, kokha silinang'ambika.


Yesu anadza natenga mkate napatsa iwo, momwemonso nsomba.


Ndipo pamene anatulukira pamtunda, anapenya moto wamakala pomwepo, ndi kansomba kosanjikikako, ndi mkate.


Pomwepo Yesu anatenga mikateyo; ndipo pamene adayamika, anagawira iwo akukhala pansi; momwemonso ndi tinsomba, monga momwe iwo anafuna.


Pali mnyamata pano, amene ali nayo mikate isanu yabarele, ndi tinsomba tiwiri; koma nanga izi zikwanira bwanji ambiri otere?