Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 19:14 - Buku Lopatulika

Koma linali tsiku lokonza Paska; panali monga ora lachisanu ndi chimodzi. Ndipo ananena kwa Ayuda, Taonani, mfumu yanu!

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma linali tsiku lokonza Paska; panali monga ora lachisanu ndi chimodzi. Ndipo ananena kwa Ayuda, Taonani, mfumu yanu!

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Linali tsiku lokonzekera chikondwerero cha Paska, ndipo nkuti nthaŵi ili ngati 12 koloko masana. Pilato adauza Ayuda kuti, “Nayitu Mfumu yanu.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Linali tsiku lokonzekera Sabata la Paska ndipo nthawi inali ora lachisanu ndi chimodzi masana. Pilato anati kwa Ayuda, “Nayi mfumu yanu.”

Onani mutuwo



Yohane 19:14
12 Mawu Ofanana  

Ndipo ora lachisanu ndi chimodzi panali mdima padziko lonse, kufikira ora lachisanu ndi chinai.


Ndipo m'mawa mwake, ndilo tsiku lotsatana ndi tsiku lokonzera, ansembe aakulu ndi Afarisi anasonkhana kwa Pilato,


Ndipo panali ora lachitatu, ndipo anampachika Iye.


Ndipo atafika tsono madzulo, popeza mpa tsiku lokonzekera, ndilo la pambuyo pa Sabata,


Ndipo ora lake pamenepo linali ngati lachisanu ndi chimodzi. Ndipo panali mdima padziko lonse kufikira ora lachisanu ndi chinai, ndipo dzuwa linada.


Ndipo panali tsiku lokonzera, ndi Sabata linayandikira.


nadza kwa Iye, nanena, Tikuoneni, mfumu ya Ayuda! Nampanda khofu.


Pomwepo ndipo anaika Yesu, chifukwa cha tsiku lokonzera la Ayuda, pakuti mandawo anali pafupi.


Pamenepo Yesu anatuluka kunja, atavala korona waminga, ndi malaya achibakuwa. Ndipo ananena nao, Taonani munthuyu!