Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 19:1 - Buku Lopatulika

Pamenepo tsono Pilato anatenga Yesu, namkwapula.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pamenepo tsono Pilato anatenga Yesu, namkwapula.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pamenepo Pilato adalamula kuti atenge Yesu ndi kumkwapula.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kenaka Pilato anatenga Yesu namukwapula mwankhanza.

Onani mutuwo



Yohane 19:1
16 Mawu Ofanana  

Olima analima pamsana panga; anatalikitsa mipere yao.


Ndinapereka msana wanga kwa omenya, ndi masaya anga kwa iwo amene anakudzula tsitsi langa; sindinabisire nkhope yanga manyazi ndi kulavulidwa.


Koma Iye analasidwa chifukwa cha zolakwa zathu, natundudzidwa chifukwa cha mphulupulu zathu; chilango chotitengera ife mtendere chinamgwera Iye; ndipo ndi mikwingwirima yake ife tachiritsidwa.


nadzampereka kwa anthu akunja kuti amnyoze ndi kumkwapula, ndi kumpachika; ndipo Iye adzaukitsidwa tsiku lachitatu.


Chifukwa cha icho, onani, ndituma kwa inu aneneri ndi anzeru ndi alembi; ena a iwo mudzawapha, mudzawapachika; ndi ena a iwo mudzawakwapula m'masunagoge mwanu, ndi kuwazunza, kuchokera kumudzi umodzi, kufikira kumudzi wina;


ndipo atamkwapula adzamupha Iye; ndipo tsiku lachitatu adzauka.


Chifukwa chake ndidzamkwapula ndi kummasula Iye.


Koma anakakamiza ndi mau okweza, napempha kuti Iye apachikidwe. Ndipo mau ao anapambana.


Kwa Ayuda ndinalandira kasanu mikwingwirima makumi anai kuperewera umodzi.


kuti akalandire kuuka koposa; koma ena anayesedwa ndi matonzo ndi zokwapulira, ndiponso nsinga, ndi kuwatsekera m'ndende;


amene anasenza machimo athu mwini yekha m'thupi mwake pamtanda, kuti ife, titafa kumachimo, tikakhale ndi moyo kutsata chilungamo; ameneyo mikwingwirima yake munachiritsidwa nayo.