Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yohane 10:21 - Buku Lopatulika

Ena ananena, Mau awa sali a munthu wogwidwa chiwanda. Kodi chiwanda chikhoza kumtsegulira maso wosaona?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ena ananena, Mau awa sali a munthu wogwidwa chiwanda. Kodi chiwanda chikhoza kumtsegulira maso wosaona?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma ena ankati, “Mau ameneŵa si a munthu wogwidwa ndi mizimu yoipa. Kodi mizimu yoipa nkupenyetsa anthu akhungu?”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Koma ena anati, “Awa si mawu a munthu wogwidwa ndi ziwanda. Kodi ziwanda zingathe bwanji kutsekula maso a wosaona?”

Onani mutuwo



Yohane 10:21
11 Mawu Ofanana  

Yehova apenyetsa osaona; Yehova aongoletsa onse owerama; Yehova akonda olungama.


Kodi Iye wakupanga khutu ngwosamva? Kodi Iye wakuumba diso ngwosapenya?


Koma Yehova ananena naye, Anampangira munthu m'kamwa ndani? Kapena analenga munthu wosalankhula ndani, kapena wogontha, kapena wamaso, kapena wakhungu? Si ndine Yehova kodi?


Pamenepo alembi anati kwa Farao, Chala cha Mulungu ichi; koma mtima wa Farao unalimba, osamvera iwo; monga adalankhula Yehova.


Khutu lakumva, ndi diso lopenya, Yehova anapanga onse awiriwo.


akhungu alandira kuona kwao, ndi opunduka miyendo ayenda, akhate akonzedwa, ndi ogontha akumva, ndi akufa aukitsidwa, ndi kwa aumphawi ulalikidwa Uthenga Wabwino.


Ndipo mbiri yake inabuka ku Siriya konse: ndipo anatengera kwa Iye onse akudwala, ogwidwa ndi nthenda ndi mazunzo a mitundumitundu, ndi ogwidwa ndi ziwanda, ndi akhunyu, ndi amanjenje; ndipo Iye anawachiritsa.


Koma kunali phwando la kukonzetsanso mu Yerusalemu; nyengoyo ndi yachisanu.


Pamene ananena izi, analavula pansi, nakanda thope ndi malovuwo, napaka thopelo m'maso,