Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yeremiya 51:3 - Buku Lopatulika

Wauta asakoke uta wake, asadzikweze m'malaya ake achitsulo; musasiye anyamata ake; muononge ndithu khamu lake lonse.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Wauta asakoke uta wake, asadzikweze m'malaya ake achitsulo; musasiye anyamata ake; muononge ndithu khamu lake lonse.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Okoka uta musaŵalekerere, kapena onyadira chovala chao chankhondo. Anyamata ake musasiyeko ndi mmodzi yemwe. Ankhondo ake onse muŵaononge.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.

Onani mutuwo



Yeremiya 51:3
12 Mawu Ofanana  

Wodala iye amene adzagwira makanda ako, ndi kuwaphwanya pathanthwe.


Mangani akavalo, bwerani, inu apakavalo, imani ndi zisoti zazitsulo; tuulani nthungo zanu, valani malaya achitsulo.


Gubani ndi kuzungulira Babiloni kumenyana naye, inu nonse okoka uta; mumponyere iye, osaderera mivi; pakuti wachimwira Yehova.


Kwera kukamenyana ndi dziko la Merataimu, ndi okhala mu Pekodi, ipha nuononge konse pambuyo pao, ati Yehova, chita monga mwa zonse ndinakuuza iwe.


Iphani ng'ombe zamphongo zake zonse; zitsikire kukaphedwa; tsoka iwo! Pakuti tsiku lao lafika, tsiku la kulanga kwao.


Ngakhale Babiloni adzakwera kumwamba, ngakhale adzalimbitsa msanje wa mphamvu yake, koma kuchokera kwa Ine akufunkha adzafika kwa iye, ati Yehova.


Pakuti imfa yakwera m'mazenera athu, yalowa m'nyumba mwathu; kuchotsa ana kubwalo, ndi anyamata kumiseu.


Pabwalo lupanga lidzalanda, ndi m'zipinda mantha; lidzaononga mnyamata ndi namwali, woyamwa pamodzi ndi munthu waimvi.


Pakuti chiweruziro chilibe chifundo kwa iye amene sanachite chifundo; chifundo chidzitamandira kutsutsana nacho chiweruziro.