Ndipo iye ananena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israele, Muuze munthuyo anakutumizani kwa ine,
Yeremiya 21:3 - Buku Lopatulika Ndipo Yeremiya anati kwa iwo, Muzitero kwa Zedekiya: Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Ndipo Yeremiya anati kwa iwo, Muzitero kwa Zedekiya: Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Koma otumidwa aja atafika, Yeremiya adaŵauza kuti, Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Koma Yehova anawuza Yeremiya kuti ayankhe Pasuri ndi Zefaniya kuti, “Kamuwuzeni Zedekiya kuti, |
Ndipo iye ananena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israele, Muuze munthuyo anakutumizani kwa ine,
nachita choipa pamaso pa Yehova Mulungu wake; sanadzichepetse kwa Yeremiya mneneri wakunena zochokera pakamwa pa Yehova.
Tifunsirenitu ife kwa Yehova; pakuti Nebukadinezara mfumu wa ku Babiloni atithira ife nkhondo; kapena Yehova adzatichitira ife monga mwa ntchito zake zolapitsa, kuti atichokere.
Yehova, Mulungu wa Israele atero, Taonani, ndidzabweza zida za nkhondo zimene zili m'manja anu, zimene mumenyana nazo ndi mfumu ya ku Babiloni, ndi Ababiloni akuzinga inu, kunja kwa malinga, ndipo ndidzazisonkhanitsa pakati pa mzinda uwu.
Pakuti Zedekiya mfumu ya Yuda inamtsekera iye, nati, Chifukwa chanji ulinkunenera, kuti, Yehova atero, Taonani, ndidzapereka mzinda uwu m'dzanja la mfumu ya Babiloni, ndipo iye adzaulanda,