Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yeremiya 18:4 - Buku Lopatulika

Ndipo pamene mbiya alikuiumba ndi dothi inaonongeka m'dzanja la woumba, anaiumbanso mbiya ina, monga kunamkomera woumba kuiumba.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pamene mbiya alikuiumba ndi dothi inaonongeka m'dzanja la woumba, anaiumbanso mbiya ina, monga kunamkomera woumba kuiumba.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chiŵiya chimene ankaumbacho chitakhala chopotoka pomalinga ndi kaumbidwe kake kolakwika, iye uja ankaumbanso chiŵiya china ndi dothi lomwelo, monga ankafunira mwiniwakeyo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Tsono amati ngati mbiya imene waumba ikhala yosawumbika bwino ankayiphwanya nʼkuwumbanso ina monga mmene afunira ndi dothi lake lomwe lija.

Onani mutuwo



Yeremiya 18:4
5 Mawu Ofanana  

Tsoka kwa iye amene akangana ndi Mlengi wake! Phale mwa mapale a dziko lapansi! Kodi dongo linganene kwa iye amene aliumba, Kodi upanga chiyani? Pena ntchito yako, Iye alibe manja?


Ndipo ndinatsikira kunyumba ya woumba, ndipo, taonani, anaumba ntchito yake ndi njinga.


Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, kuti,


Nyumba ya Israele inu, kodi sindingathe kuchita ndi inu monga woumba uyu? Ati Yehova. Taonani, monga dothi m'dzanja la woumba, momwemo inu m'dzanja langa, nyumba ya Israele.