Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yeremiya 13:7 - Buku Lopatulika

Ndipo ndinanka ku Yufurate, ndikukumba, nditenga mpango m'malo m'mene ndinaubisamo; ndipo, taonani, mpango unaonongeka, wosayenera kanthu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ndinanka ku Yufurate, ndikumba, nditenga mpango m'malo m'mene ndinaubisamo; ndipo, taonani, mpango unaonongeka, wosayenera kanthu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ine ndidapita ku Yufurate, ndipo ndidakumba pa malo amene ndidaubisa paja, nkuutenga. Koma ndidaona kuti ndi woonongeka kotheratu, wopandanso ntchito.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho ndinapita ku Yufurate kukafukula lambayo ndi kumuchotsa pamalo pamene ndinamubisa, koma nthawi imeneyi nʼkuti lambayo atawonongeka kotheratu ndipo analibenso ntchito.

Onani mutuwo



Yeremiya 13:7
10 Mawu Ofanana  

Pakuti ife tonse takhala ngati wina amene ali wosakonzeka; ndi zolungama zathu zonse zili ngati chovala chodetsedwa; ndipo ife tonse tifota monga tsamba, ndi zoipa zathu zitiuluza monga mphepo.


Anthu oipa awa, amene akana kumva mau anga, amene ayenda m'kuumirira kwa mtima wao, atsata milungu ina kuitumikira, ndi kuigwadira, adzakhala ngati mpango uwu, wosayenera kanthu.


Ndipo panali atapita masiku ambiri, kuti Yehova anati kwa ine, Uka, pita ku Yufurate, nukatenge kumeneko mpango uja, ndinakuuza iwe ukaubise kumeneko.


Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine, kuti,


onsewa apatuka, pamodzi akhala opanda pake; palibe mmodzi wakuchita zabwino, inde, palibe mmodzi ndithu.


amene kale sanakupindulire, koma tsopano watipindulira bwino iwe ndi ine;