Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yeremiya 13:4 - Buku Lopatulika

Tenga mpango umene unaugula, umene uli m'chuuno mwako, nuuke, nupite ku Yufurate, nuubise m'menemo m'phanga la m'mwala.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Tenga mpango umene unaugula, umene uli m'chuuno mwako, nuuke, nupite ku Yufurate, nuubise m'menemo m'phanga la m'mwala.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Tenga mpango uja udagula nkuvala m'chiwuno mwakowu. Unyamuke nkupita msanga ku mtsinje wa Yufurate. Kumeneko ukabise mpangowo m'ming'alu yam'mathanthwe.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Tenga lamba amene unagula ndi kuvala mʼchiwuno mwako uja. Tsono pita ku mtsinje wa Yufurate ndipo ukamubise lambayo mʼmingʼalu ya mʼmatanthwe.”

Onani mutuwo



Yeremiya 13:4
5 Mawu Ofanana  

Ku mitsinje ya ku Babiloni, kumeneko tinakhala pansi, inde tinalira, pokumbukira Ziyoni.


Ndipo mau a Yehova anadza kwa ine nthawi yachiwiri, kuti,


Imva zowawa, nuyesetse kubala, mwana wamkazi wa Ziyoni, ngati mkazi wakubala; pakuti udzatuluka m'mzinda tsopano, nudzakhala kuthengo, nudzafika ku Babiloni; komweko udzapulumutsidwa; komweko Yehova adzakuombola m'manja a adani ako.


Ndipo Yohane yekhayo anali nacho chovala chake cha ubweya wangamira, ndi lamba lachikopa m'chuuno mwake; ndi chakudya chake chinali dzombe ndi uchi wakuthengo.