Ndipo Yehoyada anachita chipangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu, akhale anthu a Yehova; pakati pa mfumunso ndi anthu.
Yeremiya 11:2 - Buku Lopatulika Imvani mau a pangano ili, nenani kwa anthu a Yuda, ndi anthu a Yerusalemu; Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Imvani mau a pangano ili, nenani kwa anthu a Yuda, ndi anthu a Yerusalemu; Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa “Imva mau a chipangano ichi, ndipo ulankhule nawo anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero “Imvani mawu a pangano ili, ndipo uwawuze anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu. |
Ndipo Yehoyada anachita chipangano pakati pa Yehova ndi mfumu ndi anthu, akhale anthu a Yehova; pakati pa mfumunso ndi anthu.
Ndipo Yehoyada anachita pangano pakati pa iye, ndi anthu onse, ndi mfumu, kuti adzakhala anthu a Yehova.
Tsono mumtima mwanga nditi ndichite chipangano ndi Yehova Mulungu wa Israele, kuti mkwiyo wake waukali utembenuke kutichokera.
Ndipo mfumu inaimirira pokhala pake, ndi kuchita pangano pamaso pa Yehova, kuti adzayenda chotsata Yehova, ndi kusunga malamulo ake, ndi mboni zake, ndi malemba ake, ndi mtima wake wonse, ndi moyo wake wonse, kuchita mau a chipangano olembedwa m'bukumu.
Ndipo tsopano, ngati mudzamvera mau anga ndithu, ndi kusunga chipangano changa, ndidzakuyesani chuma changa cha padera koposa mitundu yonse ya anthu; pakuti dziko lonse lapansi ndi langa;
Ndipo Yehova anati kwa ine, Lalikira mau onsewa m'mizinda ya Yuda, ndi m'miseu ya Yerusalemu, kuti, Tamvani mau a pangano ili, ndi kuwachita.