Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Yakobo 2:4 - Buku Lopatulika

kodi simunasiyanitse mwa inu nokha, ndi kukhala oweruza oganizira zoipa?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

kodi simunasiyanitsa mwa inu nokha, ndi kukhala oweruza oganizira zoipa?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Limenelotu ndi tsankho pakati pa inu nokhanokha, ndipo inuyo mwasanduka oweruza a maganizo oipa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

kodi simunachite tsankho pakati panu ndi kukhala oweruza a maganizo oyipa?

Onani mutuwo



Yakobo 2:4
12 Mawu Ofanana  

Taonani, ndidziwa maganizo anu, ndi chiwembu mundilingirira moipa.


Nanga kwa Iye wosasamalira nkhope za akalonga, wosasiyanitsa pakati pa wolemera ndi wosauka? Pakuti onsewo ndiwo ntchito ya manja ake.


Popeza adzaima padzanja lamanja la waumphawi, kumpulumutsa kwa iwo akuweruza koipa moyo wake.


Kodi muli chete ndithu poyenera inu kunena zolungama? Muweruza ana anthu molunjika kodi?


Mudzaweruza mosalunjika kufikira liti, ndi kusamalira nkhope ya oipa?


Chifukwa chake Inenso ndakuikani onyozeka ndi ochepseka kwa anthu onse, popeza simunasunge njira zanga, koma munaweruza mwankhope pochita chilamulo.


Ndipo Ambuye anati, Tamverani chonena woweruza wosalungama.


Musaweruze monga maonekedwe, koma weruzani chiweruziro cholungama.


Koma nzeru yochokera kumwamba iyamba kukhala yoyera, nikhalanso yamtendere, yaulere, yomvera bwino, yodzala chifundo ndi zipatso zabwino, yopanda tsankho, yosadzikometsera pamaso.


Musamanenerana, abale. Wonenera mbale, kapena woweruza mbale wake, anenera lamulo, naweruza lamulo: koma ngati uweruza lamulo, suli wochita lamulo, komatu woweruza.