Rute 4:7 - Buku Lopatulika Koma kale mu Israele pakuombola ndi pakusinthana, kutsimikiza mlandu wonse, akatero: munthu avula nsapato yake, naipereka kwa mnansi wake; ndiwo matsimikizidwe mu Israele. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Koma kale m'Israele pakuombola ndi pakusinthana, kutsimikiza mlandu wonse, akatero: munthu avula nsapato yake, naipereka kwa mnansi wake; ndiwo matsimikizidwe m'Israele. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Masiku amenewo, munthu akamachita malonda kapena kusinthana kanthu ndi mnzake, zinkayenda motere: ankavula nsapato imodzi napatsa mnzakeyo. Imeneyi ndiyo inali njira yochitira umboni m'dziko la Israele. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero (Kale mu Israeli zinkatere ngati munthu afuna kuwombola kanthu kapena kusinthana kanthu ndi mnzake kuti chikhale chakechake. Iye ankavula nsapato imodzi namupatsa mnzakeyo. Imeneyo ndiyo inali njira yochitira umboni mu Israeli). |