Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Rute 3:6 - Buku Lopatulika

Pamenepo anatsikira popunthirapo, nachita zonse monga umo mpongozi wake adamuuza.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pamenepo anatsikira popunthirapo, nachita zonse monga umo mpongozi wake adamuuza.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Choncho Rute adapita kopunthira kuja, ndipo adakachitadi monga momwe mpongozi wake uja adaamuuzira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho Rute anapita ku malo opunthirawo ndipo anachita monga momwe apongozi ake anamuwuza.

Onani mutuwo



Rute 3:6
7 Mawu Ofanana  

Estere sadawulule mtundu wake ndi chibale chake; pakuti Mordekai adamuuzitsa kuti asadziwulule.


Uzilemekeza atate wako ndi amai ako; kuti achuluke masiku ako m'dziko limene Yehova Mulungu wako akupatsa iwe.


Mwananga, tamva mwambo wa atate wako, ndi kusasiya chilangizo cha amai ako;


Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulani inu.


Amake ananena kwa atumiki, Chimene chilichonse akanena kwa inu, chitani.


Ndipo ananena naye, Zonse muzinena ndidzachita.


Ndipo atatha Bowazi kudya ndi kumwa, nusekerera mtima wake, anakagona kuthungo kwa mulu wa tirigu; nadza iye kachetechete, navundukula ku mapazi ake, nagona.