Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Rute 1:9 - Buku Lopatulika

Yehova akuloleni mupeze mpumulo yense m'nyumba ya mwamuna wake. Nawapsompsona, nakweza iwo mau ao nalira misozi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Yehova akuloleni mupeze mpumulo yense m'nyumba ya mwamuna wake. Nawapsompsona, nakweza iwo mau ao nalira misozi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Chauta akuthandizeni kuti mupeze pokhala, ndipo aliyense mwa inu akwatiwe.” Pompo adaŵampsompsona. Koma iwo adayamba kulira mokweza,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Yehova akuthandizeni kuti aliyense wa inu apeze pokhala pabwino komanso mwamuna.” Kenaka anawapsompsona koma awiriwo analira mokweza.

Onani mutuwo



Rute 1:9
8 Mawu Ofanana  

Ndipo anasendera nampsompsona; ndipo anamva kununkhira kwa zovala zake, namdalitsa, nati, Taona, kununkhira kwa mwana wanga, kufanana ndi kununkhira kwa munda anaudalitsa Yehova;


Ndipo Yakobo anampsompsona Rakele nakweza mau ake, nalira.


Ndipo sunandiloleze ine ndimpsompsone ana anga aamuna ndi aakazi? Wapusa iwe pakuchita chotero.


Ndipo anampsompsona abale ake onse, nalirira iwo; ndipo pambuyo pake abale ake onse anacheza naye.


Ndipo onsewa analira kwambiri, namkupatira Paulo pakhosi pake, nampsompsona,


Ndipo ananena naye, Iai, koma tidzapita nanu kwa anthu a kwanu.


Ndipo Naomi anati kwa apongozi ake awiri, Mukani, bwererani yense wa inu kunyumba ya amai wake; Yehova akuchitireni zokoma, monga umo munachitira akufa aja ndi ine.


Pamenepo Naomi mpongozi wake ananena naye, Mwana wanga, kodi ndisakufunire popumulako, kuti ukhale bwino?