Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Rute 1:7 - Buku Lopatulika

Natuluka iye kumene anakhalako ndi apongozi ake awiri pamodzi naye; nanka ulendo wao kubwerera ku dziko la Yuda.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Natuluka iye kumene anakhalako ndi apongozi ake awiri pamodzi naye; namka ulendo wao kubwerera ku dziko la Yuda.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Choncho adanyamuka, pamodzi ndi apongozi akewo, kuchoka kumene ankakhala kuja, nayamba ulendo wobwerera ku dziko la Yuda.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Naomi pamodzi ndi apongozi ake awiri aja anachoka kumene ankakhala ndi kuyamba ulendo obwerera kwawo ku Yuda.

Onani mutuwo



Rute 1:7
6 Mawu Ofanana  

Ndipo pakutha pake pa zaka zisanu ndi ziwirizo, mkaziyo anabwera kuchoka m'dziko la Afilisti, natuluka kukanena za nyumba yake ndi munda wake kwa mfumu.


Ndipo Mose analola mpongozi wake amuke; ndipo anachoka kunka ku dziko lake.


Ndipo ananena naye, Iai, koma tidzapita nanu kwa anthu a kwanu.


Nakweza iwo mau ao, naliranso misozi; ndi Oripa anampsompsona mpongozi wake, koma Rute anamkangamira.


Pamenepo ananyamuka iyeyu ndi apongozi ake kuti abwerere kuchoka m'dziko la Mowabu; pakuti adamva m'dziko la Mowabu kuti Yehova adasamalira anthu ake ndi kuwapatsa chakudya.


Ndipo Naomi anati kwa apongozi ake awiri, Mukani, bwererani yense wa inu kunyumba ya amai wake; Yehova akuchitireni zokoma, monga umo munachitira akufa aja ndi ine.