Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 36:9 - Buku Lopatulika

Motero cholowa cha ana a Israele sichidzanka ku fuko ndi fuko, pakuti mafuko a ana a Israele adzamamatira lonse ku cholowa chakechake.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Motero cholowa cha ana a Israele sichidzanka ku fuko ndi fuko, pakuti mafuko a ana a Israele adzamamatira lonse ku cholowa chakechake.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Choncho palibe choloŵa chimene chidzachotsedwe m'fuko lina kupatsidwa ku fuko lina. Pajatu fuko lililonse la Aisraele lidzakangamira pa choloŵa chake.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Cholowa chilichonse mu Israeli sichiyenera kupita ku fuko lina, popeza fuko lililonse la Israeli liyenera kusunga cholowa chimene linalandira.”

Onani mutuwo



Numeri 36:9
6 Mawu Ofanana  

Ndipo Naboti anati kwa Ahabu, Pali Yehova, ndi pang'ono ponse ai, kuti ndikupatseni cholowa cha makolo anga.


Monga Yehova adalamulira Mose, momwemo ana aakazi a Zelofehadi anachita;


Motero cholowa cha ana a Israele sichidzanka ku fuko ndi fuko; popeza ana a Israele adzamamatira yense ku cholowa cha fuko la makolo ake.


Ndipo mwana wamkazi yense wa mafuko a ana a Israele, wakukhala nacho cholowa, akwatibwe ndi wina wa banja la fuko la kholo lake, kuti ana a Israele akhale nacho yense cholowa cha makolo ake.


Pamenepo Yoswa anauza anthu amuke, yense ku cholowa chake.


Chifukwa chake mbuye wanga mfumu amvere mau a kapolo wake. Ngati ndi Yehova anakuutsirani inu kutsutsana ndi ine, alandire chopereka; koma ngati ndi ana a anthu, atembereredwe pamaso pa Yehova, pakuti anandipirikitsa lero kuti ndisalandireko cholowa cha Yehova, ndi kuti, Muka, utumikire milungu ina.