Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 35:2 - Buku Lopatulika

Uza ana a Israele, kuti apatseko Alevi cholowa chaochao, mizinda yokhalamo; muwapatsenso Alevi mabusa akuzungulira mizinda.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Uza ana a Israele, kuti apatseko Alevi cholowa chaochao, midzi yokhalamo; muwapatsenso Alevi mabusa akuzungulira midzi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Ulamule Aisraele kuti pa choloŵa chaocho, apatseko Alevi mizinda yoti azikhalamo. Ndipo Aleviwo muŵapatsenso mabusa pozungulira mizindayo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Lamula Aisraeli kuti apereke kwa Alevi midzi yoti azikhalamo kuchokera pa cholowa chomwe adzalandira. Muwapatsenso malo oweteramo ziweto kuzungulira midziyo.

Onani mutuwo



Numeri 35:2
14 Mawu Ofanana  

Ndipo Davide anati kwa msonkhano wonse wa Israele, Chikakomera inu, ndipo chikachokera kwa Yehova Mulungu wathu, titumize konse kuti abale athu otsala m'dziko lonse la Israele, ndi ansembe ndi Alevi okhala nao m'mizinda yao yokhala napo podyetsa, kuti asonkhane kwa ife;


Pakuti Alevi anasiya podyetsa pao, ndi maiko aoao, nadza ku Yuda ndi ku Yerusalemu; popeza Yerobowamu ndi ana ake anawataya, kuti asachitire Yehova ntchito ya nsembe;


panalinso amuna mwa ana a Aroni ansembe, okhala m'minda ya kubusa kwa mizinda yao, m'mzinda uliwonse, otchulidwa maina ao, agawire amuna onse mwa ansembe, ndi onse mwa Alevi, oyesedwa mwa chibadwidwe magawo ao.


Ndinazindikiranso kuti sanapereke kwa Alevi magawo ao; m'mwemo Alevi ndi oimbira adathawira yense kumunda wake.


Kuyambira tsono dziko la Alevi kufikira dziko la mzinda, ndiwo a pakati pa magawo ake a kalonga, pakati pa malire a Yuda ndi malire a Benjamini, kukhale kwa kalonga.


Ndi m'malire a Yuda, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo, pakhale chopereka muchipereke, mikono zikwi makumi awiri mphambu zisanu kupingasa kwake, ndi m'litali mwake lilingane ndi magawo enawo, kuyambira mbali ya kum'mawa kufikira mbali ya kumadzulo; ndi malo opatulika akhale pakati pake.


Ndipo Yehova ananena ndi Mose m'zidikha za Mowabu, pa Yordani, ku Yeriko, ndi kuti,


Ndipo mizinda ndiyo yokhalamo iwowa; ndi mabusa akhale a ng'ombe zao, ndi zoweta zao, inde nyama zao zonse.


Ndipo Mlevi akachokera kumudzi wanu wina mu Israele monse, kumene akhalako, nakadza ndi chifuniro chonse cha moyo wake ku malo amene Yehova adzasankha;