Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 20:19 - Buku Lopatulika

Ndipo ana a Israele ananena naye, Tidzatsata mseu; ndipo tikakamwa madzi ako, ine ndi zoweta zanga, pamenepo ndidzapatsa mtengo wake; sindifuna kanthu kena koma kungopitapo mwa njira.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ana a Israele ananena naye, Tidzatsata mseu; ndipo tikakamwa madzi ako, ine ndi zoweta zanga, pamenepo ndidzapatsa mtengo wake; sindifuna kanthu kena koma kungopitapo mwa njira.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Aisraele adamuuza kuti, “Ife tidzangodzera mu mseu waukulu mokhamo. Ngati ife ndi zoŵeta zathu timwako madzi anu, tidzalipira. Mungotilola kuti tidutse chabe.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Aisraeli anayankha kuti, “Tidzayenda motsata msewu waukulu. Ndipo ngati ife kapena ziweto zathu tidzamwa madzi anu tidzalipira. Tikungofuna tidutse nawo, palibenso china.”

Onani mutuwo



Numeri 20:19
4 Mawu Ofanana  

Ndipo anthu ambiri osokonezeka anakwera nao; ndi nkhosa ndi ng'ombe, zoweta zambirimbiri.


Undigulitse chakudya ndi ndalama, kuti ndidye; ndi kundipatsa madzi kwa ndalama, kuti ndimwe; chokhachi ndipitire choyenda pansi;


Mugulane nao chakudya ndi ndalama, kuti mudye; mugulane naonso madzi kuti mumwe.


Ndipo ng'ombezo zinatsata njira yolunjika ku Betesemesi, zinali kuyenda mumseu, zilikulira; sizinapatukire ku dzanja lamanja, kapena kulamanzere; ndipo mafumu a Afilisti anazitsatira kufikira ku malire a Betesemesi.