Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 15:38 - Buku Lopatulika

Nena ndi ana a Israele, nuwauze kuti adziombere mphonje m'mphepete mwa zovala zao, mwa mibadwo yao, naike pamphonje m'mphepetemo thonje lamadzi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Nena ndi ana a Israele, nuwauze kuti adziombere mphonje m'mphepete mwa zovala zao, mwa mibadwo yao, naike pamphonje m'mphepetemo thonje lamadzi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

“Lankhula ndi Aisraele, ndipo uŵauze kuti pa mibadwo yao yonse azisokerera mphonje pa ngodya za zovala, ndipo pa mphonje ya ngodya iliyonse asokerepo chingwe chobiriŵira.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

“Yankhula ndi Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Pa mibado yanu yonse muzisokerera mphonje pa ngodya za zovala zanu ndipo pa ngodya ya mphonje iliyonse azisokererapo chingwe chobiriwira.

Onani mutuwo



Numeri 15:38
5 Mawu Ofanana  

Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,


Koma amachita ntchito zao zonse kuti aonekere kwa anthu; pakuti akulitsa chitando chake cha njirisi zao, nakulitsa mphonje,


Ndipo onani, mkazi, anali ndi nthenda yachidwalire zaka khumi ndi ziwiri, anadza pambuyo pake, nakhudza mphonje ya chofunda chake;


anadza pambuyo pake, nakhudza mphonje ya chovala chake; ndipo pomwepo nthenda yake inaleka.


Mudzipangire mphonje pangodya zinai za chofunda chanu chimene mudzifunda nacho.