Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 14:39 - Buku Lopatulika

Ndipo Mose anauza ana a Israele mau onse awa; ndipo anthu anamva chisoni chambiri.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo Mose anauza ana a Israele mau onse awa; ndipo anthu anamva chisoni chambiri.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mose adaŵafotokozera Aisraele mau onseŵa, ndipo anthu adalira kwambiri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mose atafotokoza izi kwa Aisraeli onse, anthuwo analira kwambiri.

Onani mutuwo



Numeri 14:39
8 Mawu Ofanana  

Ndipo pamene anthu anamva mau awa oipa anachita chisoni; ndipo panalibe mmodzi anavala zokometsera zake.


Utsiru wa munthu ukhotetsa njira yake; mtima wake udandaula pa Yehova.


Yehova, iwo adza kwa Inu movutika, iwo anathira pemphero, muja munalikuwalanga.


Nunene nao, Pali Ine ati Yehova, ndidzachitira inu ndithu monga mwanena m'makutu mwanga;


Koma Yoswa mwana wa Nuni, ndi Kalebe mwana wa Yefune, anakhala ndi moyo mwa amuna aja adamukawo kukazonda dziko.


koma anawo a Ufumu adzatayidwa kumdima wakunja; komweko kudzakhala kulira ndi kukukuta mano.


Pakuti mudziwa kutinso pamene anafuna kulowa dalitsolo, anakanidwa (pakuti sanapeze malo akulapa), angakhale analifunafuna ndi misozi.


Mwa ichi ana a Israele sangathe kuima pamaso pa adani ao, awafulatira adani ao, pakuti aperekedwa aonongeke. Sindidzakhalanso nanu mukapanda kuononga choperekedwacho, kuchichotsa pakati pa inu.