Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Numeri 10:28 - Buku Lopatulika

Potero maulendo a ana a Israele anakhala monga mwa magulu ao; nayenda ulendo wao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Potero maulendo a ana a Israele anakhala monga mwa magulu ao; nayenda ulendo wao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Umenewu ndiwo mndandanda wa kayendedwe ka Aisraele, pamene ankanyamuka ulendo wao m'magulumagulu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Umenewu ndiwo unali mndandanda wa kayendedwe ka magulu a Aisraeli pamene ankanyamuka ulendo wawo mʼmagulumagulu.

Onani mutuwo



Numeri 10:28
9 Mawu Ofanana  

Nati, Ndaniyo atuluka ngati mbandakucha, wokongola ngati mwezi, woyera ngati dzuwa, woopsa ngati nkhondo ndi mbendera?


Ndi pa gulu la fuko la ana a Nafutali anayang'anira Ahira mwana wa Enani.


Ndipo Mose anati kwa Hobabu mwana wa Reuwele Mmidiyani mpongozi wa Mose, Ife tili kuyenda kunka ku malo amene Yehova anati, Ndidzakupatsani awa; umuke nafe, tidzakuchitira zokoma; popeza Yehova wanenera Israele zokoma.


Ndipo ana a Israele anachita monga mwa zonse Yehova adauza Mose, momwemo anamanga mahema ao pa mbendera zao, momwemonso anayenda paulendo, yense monga mwa mabanja ake, monga mwa nyumba za makolo ake.


pakuti Mulungu sali Mulungu wa chisokonezo koma wa mtendere; monga mwa Mipingo yonse ya oyera mtima.


Koma zonse zichitike koyenera ndi kolongosoka.


Pakuti ndingakhale ndili kwina m'thupi, komatu mumzimu ndili pamodzi ndi inu, wokondwera pakupenya makonzedwe anu, ndi chilimbiko cha chikhulupiriro chanu cha kwa Khristu.