Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Nehemiya 6:3 - Buku Lopatulika

Ndipo ndinawatumizira mithenga, ndi kuti, Ndilikuchita ntchito yaikulu, sindingathe kutsika; ndiidulirenji padera ntchito poileka ine, ndi kukutsikirani?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo ndinawatumizira mithenga, ndi kuti, Ndilikuchita ntchito yaikulu, sindikhoza kutsika; ndiidulirenji padera ntchito poileka ine, ndi kukutsikirani?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nchifukwa chake ndidaŵatumira amithenga kukaŵauza kuti, “Ine kuno ndili pa ntchito yaikulu, sindingathe kuchoka kuti ndibwere kumeneko. Kodi ntchito iime, pofuna kuti ndibwere kumeneko?”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”

Onani mutuwo



Nehemiya 6:3
9 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake ndinawaika potera m'kati mwa linga, popenyeka; inde ndinaika anthu monga mwa mabanja ao, akhale nao malupanga ao, nthungo zao, ndi mauta ao.


anatumiza mau kwa ine Sanibalati ndi Gesemu, kuti, Tiyeni tikomane kumidzi ya ku Chigwa cha Ono; koma analingirira za kundichitira choipa.


Nanditumizira ine mau otere kanai; ndinawabwezeranso mau momwemo.


Wachibwana akhulupirira mau onse; koma wochenjera asamalira mayendedwe ake.


Chilichonse dzanja lako lichipeza kuchichita, uchichite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe ntchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.


Taonani, Ine ndikutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu; chifukwa chake khalani ochenjera monga njoka, ndi oona mtima monga nkhunda.


ndi kunena kuti, Munthu uyu anayamba kumanga, koma sanathe kumaliza.


Tiyenera kugwira ntchito za Iye wondituma Ine, pokhala pali msana; ukudza usiku pamene palibe munthu angakhoze kugwira ntchito.