Nehemiya 3:31 - Buku Lopatulika Potsatizana naye anakonza Malikiya wina wa osula golide kufikira kunyumba ya antchito a m'kachisi, ndi ya ochita malonda, pandunji pa Chipata cha Hamifikadi, ndi kuchipinda chosanja cha kungodya. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Potsatizana naye anakonza Malikiya wina wa osula golide kufikira kunyumba ya Anetini, ndi ya ochita malonda, pandunji pa chipata cha Hamifikadi, ndi kuchipinda chosanja cha kungodya. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Pambali pa iyeyo Malikiya, mmodzi mwa amisiri a golide, adakonza chigawo china mpaka kukafika ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu, ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda. Chigawo chimenechi chidaayang'anana ndi Chipata cha Mifikada, kufikira ku chipinda chapamwamba chapangodya. Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Motsatana naye, Malikiya mmodzi mwa amisiri a golide anakonza chigawo china mpaka ku nyumba ya atumiki a ku Nyumba ya Mulungu ndiponso ku nyumba ya anthu amalonda moyangʼanana ndi chipata cha Mifikade ndiponso mpaka pa chipinda chapamwamba chapangodya. |
Potsatizana naye Hananiya mwana wa Selemiya, ndi Hanuni mwana wachisanu ndi chimodzi wa Zalafi, anakonza gawo lina. Potsatizana naye anakonza Mesulamu mwana wa Berekiya pandunji pa chipinda chake.
Ndi pakati pa chipinda chosanja cha kungodya ndi Chipata cha Nkhosa anakonza osula golide ndi ochita malonda.
Pambali pake anakonza Uziyele mwana wa Haraya, wa iwo osula golide. Ndi padzanja pake anakonza Hananiya, wa iwo osanganiza zonunkhira; nalimbikitsa Yerusalemu mpaka linga lachitando.