Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Nehemiya 3:24 - Buku Lopatulika

Potsatizana naye Binuyi mwana wa Henadadi anakonza gawo lina, kuyambira kunyumba ya Azariya kufikira popindirira kufikira kungodya.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Potsatizana naye Binuyi mwana wa Henadadi anakonza gawo lina, kuyambira kunyumba ya Azariya kufikira popindirira kufikira kungodya.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pambali pa iyeyo Binuyi, mwana wa Henadadi, adakonza chigawo china, kuyambira ku nyumba ya Azariya mpaka kukafika ku Ndonyo,

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Motsatana naye, Binuyi mwana wa Henadadi anakonzanso chigawo china, kuchokera pa nyumba ya Azariya kukafika potsirizira pa ngodya.

Onani mutuwo



Nehemiya 3:24
7 Mawu Ofanana  

Pamenepo anaimirira pamodzi Yesuwa ndi ana ake ndi abale ake, Kadimiyele ndi ana ake, ana a Yuda, kuyang'anira ogwira ntchito m'nyumba ya Mulungu, ana a Henadadi ndi ana ao ndi abale ao Alevi.


ndi abale ao: Sebaniya, Hodiya, Kelita, Pelaya, Hanani,


Ndi Alevi ndiwo Yesuwa mwana wa Azaniya, Binuyi wa ana a Henadadi, Kadimiyele;


Malikiya mwana wa Harimu, ndi Hasubu mwana wa Pahatimowabu, anakonza gawo lina, ndi Nsanja ya Ng'anjo.


Ndi pa mbali pake Ezere mwana wa Yesuwa, mkulu wa Mizipa, anakonza gawo lina, pandunji pokwerera kunyumba yosungamo zida za nkhondo, popindirira linga.


Potsatizana nao anakonza Benjamini ndi Hasubu pandunji pa nyumba pao. Potsatizana nao anakonza Azariya mwana wa Maaseiya mwana wa Ananiya pafupi pa nyumba yake.


Potsatizana nao Atekowa anakonza gawo lina, pandunji pa nsanja yaikulu yosomphoka ndi kulinga la Ofele.