Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Nehemiya 3:20 - Buku Lopatulika

Potsatizana naye Baruki mwana wa Zabai anafulumira kukonza gawo lina kuyambira popindirira mpaka kukhomo la nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Potsatizana naye Baruki mwana wa Zabai anafulumira kukonza gawo lina kuyambira popindirira mpaka kukhomo la nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pambali pa iyeyo Baruki mwana wa Zabai adakonza chigawo kuyambira pa Ndonyo mpaka ku chitseko cha nyumba ya Eliyasibu, mkulu wa ansembe.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Motsatana naye, Baruki mwana wa Zakai anakonzanso chigawo china kuchokera pa ngodya mpaka pa chitseko cha nyumba ya Eliyasibu mkulu wa ansembe.

Onani mutuwo



Nehemiya 3:20
9 Mawu Ofanana  

Ndi a ana a Bebai: Yehohanani, Hananiya, Zabai, Atilai.


Daniele, Ginetoni, Baruki,


Koma wina wa ana a Yehoyada, mwana wa Eliyasibu mkulu wa ansembe, anali mkamwini wa Sanibalati Muhoroni; chifukwa chake ndinampirikitsa kumchotsa kwa ine.


Chinkana ichi, Eliyasibu wansembe, woikidwa asunge zipinda za nyumba ya Mulungu wathu, anachita chibale ndi Tobiya,


Pamenepo Eliyasibu mkulu wa ansembe ananyamuka pamodzi ndi abale ake ansembe, namanga Chipata cha Nkhosa; anachipatula, naika zitseko zake, inde anachipatula mpaka Nsanja ya Zana, mpaka Nsanja ya Hananele.


Potsatizana naye Meremoti mwana wa Uriya mwana wa Hakozi anakonza gawo lina, kuyambira kukhomo la nyumba ya Eliyasibu kufikira malekezero ake a nyumba ya Eliyasibu.


Chilichonse dzanja lako lichipeza kuchichita, uchichite ndi mphamvu yako; pakuti mulibe ntchito ngakhale kulingirira ngakhale kudziwa, ngakhale nzeru, kumanda ulikupitako.


musakhale aulesi m'machitidwe anu; khalani achangu mumzimu, tumikirani Ambuye;