Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Nehemiya 3:11 - Buku Lopatulika

Malikiya mwana wa Harimu, ndi Hasubu mwana wa Pahatimowabu, anakonza gawo lina, ndi Nsanja ya Ng'anjo.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Malikiya mwana wa Harimu, ndi Hasubu mwana wa Pahatimowabu, anakonza gawo lina, ndi Nsanja ya Ng'anjo.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Malikiya, mwana wa Harimu, ndiponso Hasubu mwana wa Pahatimowabu, adakonza chigawo china pamodzi ndi Nsanja ya Ng'anjo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Malikiya mwana wa Harimu ndi Hasubu mwana wa Pahati-Mowabu anakonzanso chigawo china ndiponso Nsanja ya Ngʼanjo.

Onani mutuwo



Nehemiya 3:11
10 Mawu Ofanana  

Ndi a ana a Harimu: Eliyezere, Isiya, Malikiya, Semaya, Simeoni,


Ana a Pahatimowabu, a ana a Yesuwa ndi Yowabu, zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi atatu kudza khumi ndi awiri.


Wa ana a Pahatimowabu, Eliehoenai mwana wa Zerahiya; ndi pamodzi naye amuna mazana awiri.


Akulu a anthu: Parosi, Pahatimowabu, Elamu, Zatu, Bani,


Harimu, Meremoti, Obadiya,


Ndi gulu lina la oyamikira linamuka mokomana nao, ndi ine ndinawatsata, pamodzi ndi limodzi la magawo awiri la anthu palinga, napitirira pa Nsanja ya Ng'anjo, mpaka kulinga lachitando;


Ndi pambali pao anakonza Yedaya mwana wa Harumafa, pandunji pa nyumba yake. Ndi pambali pake anakonza Hatusi mwana wa Hasabineya.


Ana a Pahatimowabu, a ana a Yesuwa ndi Yowabu, zikwi ziwiri mphambu mazana asanu ndi atatu kudza khumi limodzi ndi asanu ndi atatu.


Ana a Harimu, mazana atatu mphambu makumi awiri.


Zungulirani Ziyoni, ndipo muuzinge, werengani nsanja zake.