Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Nehemiya 13:11 - Buku Lopatulika

Potero ndinatsutsana nao olamulira, ndinati, Yasiyidwiranji nyumba ya Mulungu? Ndipo ndinawasonkhanitsa, ndi kuwaika m'malo mwao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Potero ndinatsutsana nao olamulira, ndinati, Yasiyidwiranji nyumba ya Mulungu? Ndipo ndinawasonkhanitsa, ndi kuwaika m'malo mwao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Choncho ndidaŵadzudzula akuluakulu aja kuti, “Kodi chifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa chonchi?” Ndipo ndidasonkhanitsa anthu aja ndi kuŵaikanso pa ntchito zimene ankazigwira

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Choncho ndinadzudzula akuluakulu aja ndipo ndinawafunsa kuti, “Nʼchifukwa chiyani Nyumba ya Mulungu yasiyidwa?” Ndipo ine ndinawayitanitsa pamodzi ndi kuwayika mʼmalo awo.

Onani mutuwo



Nehemiya 13:11
8 Mawu Ofanana  

Pakuti ana a Israele ndi ana a Levi, azibwera nayo nsembe yokweza yatirigu, ndi yavinyo ndi yamafuta, kuzipinda kuli zipangizo za malo opatulika, ndi ansembe akutumikira, ndi odikira, ndi oimbira; kuti tisasiye nyumba ya Mulungu wathu.


Pamenepo ndinatsutsana nao aufulu a Yuda, ndinanena nao, Chinthu chanji choipa ichi muchichita, ndi kuipsa nacho tsiku la Sabata?


Ndipo ndinatsutsana nao, ndi kuwatemberera, ndi kukantha ena a iwo, ndi kumwetula tsitsi lao, ndi kuwalumbiritsa pa Mulungu ndi kuti, Musapereke ana anu aakazi kwa ana ao aamuna, kapena kutengera ana anu aamuna, kapena a inu nokha, ana ao aakazi.


popeza ndinaopa unyinji waukulu, ndi chipepulo cha mafuko chinandiopsetsa; potero ndinakhala chete osatuluka pakhomo panga.


Omwe asiya chilamulo atama oipa; koma omwe asunga chilamulo akangana nao.


Ndipo zoipa za anyamatawo zinali zazikulu ndithu pamaso pa Yehova; pakuti anthu anaipidwa ndi nsembe ya Yehova.