Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mlaliki 5:9 - Buku Lopatulika

Phindutu la dziko lipindulira onse; ngakhale mfumu munda umthandiza;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Phindutu la dziko lipindulira onse; ngakhale mfumu munda umthandiza;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Alimi onse amatengako dzinthu dzam'minda, koma ndi mfumu yokha imene imaona phindu lake la mindayo.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Anthu onse amatengako zokolola za mʼminda: koma ndi mfumu yokha imene imapeza phindu la mindayi.

Onani mutuwo



Mlaliki 5:9
15 Mawu Ofanana  

Kunena za kumwamba, kumwamba ndiko kwa Yehova; koma dziko lapansi analipereka kwa ana a anthu.


M'kulima kwa osauka muli zakudya zambiri; koma zinazo zimaonongeka posowa chiweruzo.


Wolima munda wake zakudya zidzamkwanira; koma wotsata anthu opanda pake umphawi udzamkwanira.


Pali mmodzi palibe wachiwiri; inde, alibe mwana ngakhale mbale; koma ntchito yake yonse ilibe chitsiriziro, ngakhale diso lake silikhuta chuma. Samati, Ndigwira ntchito ndi kumana moyo wanga zabwino chifukwa cha yani? Ichinso ndi chabe, inde, vuto lalikulu.


Wokonda siliva sadzakhuta siliva; ngakhale wokonda chuma sadzakhuta phindu; ichinso ndi chabe.


Ukaona anthu alikutsendereza aumphawi, ndi kuchotsa chilungamo ndi chiweruzo mwachiwawa pa dera lina la dziko, usazizwepo; pakuti mkulu wopambana asamalira; ndipo alipo akulu ena oposa amenewo.


Ntchito zake zonse munthu angogwirira m'kamwa mwake, koma mtima wake sukhuta.