Mlaliki 4:7 - Buku Lopatulika Pamenepo ndinabwera ndi kupenyera zachabe kunja kuno. Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014 Pamenepo ndinabwera ndi kupenyera zachabe kunja kuno. Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa Ndidazindikira chinanso chopanda phindu pansi pano: Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero Ndinaonanso chinthu china chopanda phindu pansi pano: |
Ndinabweranso tsono ndi kupenyera nsautso zonse zimachitidwa kunja kuno; ndipo taona, misozi ya otsenderezedwa, koma analibe wakuwatonthoza; ndipo akuwatsendereza anali ndi mphamvu koma iwowa analibe wakuwatonthoza.
Dzanja limodzi lodzala pali mtendere liposa manja awiri oti thoo pali vuto ndi kungosautsa mtima.
Pali mmodzi palibe wachiwiri; inde, alibe mwana ngakhale mbale; koma ntchito yake yonse ilibe chitsiriziro, ngakhale diso lake silikhuta chuma. Samati, Ndigwira ntchito ndi kumana moyo wanga zabwino chifukwa cha yani? Ichinso ndi chabe, inde, vuto lalikulu.
Koma mau anga ndi malemba anga, amene ndinalamulira atumiki anga aneneriwo, kodi sanawapeze makolo anu? Ndipo anabwera, nati, Monga umo Yehova wa makamu analingirira kutichitira ife, monga mwa njira zathu ndi monga mwa machitidwe athu, momwemo anatichitira.