Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mlaliki 12:3 - Buku Lopatulika

tsikulo omwe asunga nyumba adzanthunthumira, amuna olimba nadzawerama, akupera nadzaleka poperewera, omwe ayang'ana pamazenera nadzadetsedwa;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

tsikulo omwe asunga nyumba adzanthunthumira, amuna olimba nadzawerama, akupera nadzaleka poperewera, omwe ayang'ana pamazenera nadzadetsedwa;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Nthaŵi imeneyo miyendo yako izidzanjenjemera, manja ako adzafooka. Mano ako oŵerengekawo azidzalephera nkutafuna komwe, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nthawi imene manja ako adzanjenjemera, miyendo yako idzafowoka, pamene mano ako adzalephera kutafuna chifukwa ndi owerengeka, ndipo maso ako adzayamba kuchita chidima.

Onani mutuwo



Mlaliki 12:3
9 Mawu Ofanana  

Ndipo panali atakalamba Isaki, ndi maso ake anali akhungu losaona nalo, anamuitana Esau mwana wake wamwamuna wamkulu, nati kwa iye, Mwana wanga; ndipo anati kwa iye, Ndine pano.


Koma maso a Israele anali akhungu mu ukalamba wake, ndipo sanathei kuona. Ndipo anadza nao pafupi; ndipo anapsompsona iwo, nawafungatira.


Iye analanda mphamvu yanga panjira; anachepsa masiku anga.


Ndakhala ine monga ngati iye anali bwenzi langa, kapena mbale wanga; polira ndinaweramira pansi, monga munthu wakulira maliro amai wake.


Ndapindika, ndawerama kwakukulu; ndimayenda woliralira tsiku lonse.


Atero Yehova wa makamu: M'miseu ya Yerusalemu mudzakhalanso amuna ndi akazi okalamba, yense ndi ndodo yake m'dzanja lake chifukwa cha ukalamba wake.


Ndipo kunali nthawi yomweyo Eli atagona m'malo mwake (maso ake anayamba chizirezire osatha kupenya bwino);