Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mlaliki 11:7 - Buku Lopatulika

Indetu kuunika nkokoma, maso napeza bwino m'kuona dzuwa.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Indetu kuunika nkokoma, maso napeza bwino m'kuona dzuwa.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kuŵala kwam'maŵa kumasangalatsa, ndipo maso ako akaona dzuŵa amakondwa.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kuwala nʼkwabwino, ndipo maso amasangalala kuona dzuwa.

Onani mutuwo



Mlaliki 11:7
10 Mawu Ofanana  

Koma anandiombola ndingatsikire kumanda, ndi moyo wanga udzaona kuunika.


kumbweza angalowe kumanda, kuti kuunika kwa moyo kumuwalire.


Pakuti mwalanditsa moyo wanga kuimfa, simunatero nao mapazi anga kuti ndingagwe? Kuti ndiyende pamaso pa Mulungu m'kuunika kwa amoyo.


Pakuti Yehova Mulungu ndiye dzuwa ndi chikopa; Yehova adzapatsa chifundo ndi ulemerero; sadzakaniza chokoma iwo akuyenda angwiro.


Kuunika kwa maso kukondweretsa mtima; ndipo pomveka zabwino mafupa amatenga uwisi.


Waumphawi ndi wotsendereza akumana; Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.


ngakhale lisanade dzuwa, ndi kuunika, ndi mwezi, ndi nyenyezi, mitambo ndi kubweranso italeka mvula;


Ngakhale dzuwa siliona ngakhale kulidziwa, imeneyi ipambana winayo kupuma;


Nzeru ili yabwino pamodzi ndi cholowa; akuona dzuwa apindula nayo.


kotero kuti mukakhale ana a Atate wanu wa Kumwamba; chifukwa Iye amakwezera dzuwa lake pa oipa ndi pa abwino, namavumbitsira mvula pa olungama ndi pa osalungama.