Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mlaliki 1:1 - Buku Lopatulika

Mau a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya mu Yerusalemu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mau a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya m'Yerusalemu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Naŵa mau a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mawu a Mlaliki, mwana wa Davide, mfumu ya ku Yerusalemu:

Onani mutuwo



Mlaliki 1:1
13 Mawu Ofanana  

Ndipo Solomoni anakhala mfumu ya Israele yense mu Yerusalemu zaka makumi anai.


Ndiponso waika aneneri akubukitsa za iwe ku Yerusalemu, ndi kuti, Ku Yuda kuli mfumu, ndipo zidzamveka kwa mfumu, kuti kuli zotere. Tiyeni tsono tipangane pamodzi.


Ndalalikira chilungamo mu msonkhano waukulu; onani, sindidzaletsa milomo yanga, mudziwa ndinu Yehova.


Miyambo ya Solomoni mwana wa Davide, mfumu ya Israele.


Mumpatse zipatso za manja ake; ndi ntchito zake zimtame kubwalo.


Ine Mlaliki ndinali mfumu ya Israele mu Yerusalemu.


Taonani, ichi ndachipeza, ati Mlalikiyo, m'kuphatikiza chinthu china ndi chinzake, ndikazindikire malongosoledwe ao;


Mzimu wa Ambuye Yehova uli pa ine; pakuti Yehova wandidzoza ine ndilalikire mau abwino kwa ofatsa; Iye wanditumiza ndikamange osweka mtima, ndikalalikire kwa am'nsinga mamasulidwe, ndi kwa omangidwa kutsegulidwa kwa m'ndende;


Nyamuka, pita ku Ninive mzinda waukulu uja, nuulalikire uthenga umene ndikuuza.


ndipo sanalekerere dziko lapansi lakale, koma anasunga Nowa mlaliki wa chilungamo, ndi anzake asanu ndi awiri, pakulitengera dziko la osapembedza chigumula;