Mika 1:7 - Buku Lopatulika
Ndi mafano ake osema onse adzaphwanyika, ndi mphotho zake zonse zidzatenthedwa ndi moto, ndi mafano ake onse ndidzawapasula; pakuti anazisonkhanitsa pa mphotho ya mkazi wachiwerewere, ndipo zidzabwerera kumphotho ya mkazi wachiwerewere.
Onani mutuwo
Ndi mafano ake osema onse adzaphwanyika, ndi mphotho zake zonse zidzatenthedwa ndi moto, ndi mafano ake onse ndidzawapasula; pakuti anazisonkhanitsa pa mphotho ya mkazi wachiwerewere, ndipo zidzabwerera kumphotho ya mkazi wachiwerewere.
Onani mutuwo
Mafano ake onse ndidzaŵaphwanyaphwanya, ndipo mitulo yake yonse idzatenthedwa m'moto. Zithunzi zonse za milungu yake ndidzaziwononga. Mphatso zake adazilandira kuchokera ku malipiro a akazi adama, choncho enanso adzazigwiritsa ntchito ngati malipiro a akazi adama.”
Onani mutuwo
Mafano ake onse ndidzawaphwanyaphwanya; mphatso zake zonse ndidzazitentha ndi moto; ndidzawononga zifanizo zonse za milungu yake. Popeza analandira mphatso zake kuchokera ku malipiro a akazi achiwerewere, mphatsozonso zidzagwiritsidwa ntchito ndi ena ngati malipiro a akazi achiwerewere.”
Onani mutuwo