Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mika 1:15 - Buku Lopatulika

Ndidzakutengeranso wokhala mu Maresa iwe, iye amene adzakulandira ukhale cholowa chake; ulemerero wa Israele udzafikira ku Adulamu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndidzakutengeranso wokhala m'Maresa iwe, iye amene adzakulandira ukhale cholowa chake; ulemerero wa Israele udzafikira ku Adulamu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inunso anthu a ku Maresa, ndidzakutumirani adani kuti akugonjetseni. Akuluakulu a ku Israele adzabisala m'thanthwe la Adulamu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndidzabweretsa mgonjetsi kudzalimbana ndi inu okhala mu Maresa. Ulemerero wa Israeli udzafika ku Adulamu.

Onani mutuwo



Mika 1:15
11 Mawu Ofanana  

Ndipo panali nthawi yomweyo, kuti Yuda anatsikira kwa abale ake nalowa kwa Mwadulamu, dzina lake Hira.


Ndipo atatu a mwa makamu atatu opambanawo, anatsika nafika kwa Davide nyengo ya kukolola m'phanga la ku Adulamu; ndi gulu la Afilisti linamanga zithando m'chigwa cha Refaimu.


ndi Betezuri, ndi Soko, ndi Adulamu,


Ndipo mudzachita chiyani tsiku lakudza woyang'anira, ndi chipasuko chochokera kutali? Mudzathawira kwa yani kufuna kuthangatidwa? Mudzasiya kuti ulemerero wanu?


Za ana a Amoni. Yehova atero: Kodi Israele alibe ana aamuna? Alibe wolowa dzina? M'mwemo mfumu yao yalowa pa Gadi chifukwa chanji, ndi anthu ake akhala m'mizinda mwake?


mfumu ya ku Libina, imodzi; mfumu ya ku Adulamu, imodzi;


Yaramuti, ndi Adulamu, Soko, ndi Azeka;


ndi Keila ndi Akizibu, ndi Maresa; mizinda isanu ndi inai pamodzi ndi midzi yao.


Motero Davide anachoka kumeneko, napulumukira ku phanga la ku Adulamu; ndipo pamene abale ake ndi banja lonse la atate wake anamva, iwo anatsikira kumeneko kwa iye.