Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 8:30 - Buku Lopatulika

Ndipo panali patali ndi iwo gulu la nkhumba zambiri zilinkudya.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo panali patali ndi iwo gulu la nkhumba zambiri zilinkudya.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pafupi pomwepo pankadya gulu lalikulu la nkhumba.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo patali pake panali gulu la nkhumba zimene zimadya.

Onani mutuwo



Mateyu 8:30
10 Mawu Ofanana  

Wakupha ng'ombe alingana ndi wakupha munthu; iye wapereka nsembe ya mwanawankhosa alingana ndi wothyola khosi la galu; wothira nsembe yaufa akunga wothira mwazi wa nkhumba; wofukiza lubani akunga wodalitsa fano; inde iwo asankha njira zaozao, ndipo moyo wao ukondwerera m'zonyansa zao;


Ndi nkhumba, popeza igawanika chiboda, nikhala yogawanikadi chiboda, koma yosabzikula, muiyese yodetsedwa.


Musamapatsa chopatulikacho kwa agalu, ndipo musamaponya ngale zanu patsogolo pa nkhumba, kuti zingazipondereze ndi mapazi ao, ndi potembenuka zingang'ambe inu.


Ndipo onani, anafuula nati, Tili nanu chiyani, Inu Mwana wa Mulungu? Mwadza kuno kodi kutizunza ife, nthawi yake siinafike?


Ndipo mizimuyo inampempha Iye ninena, Ngati mutitulutsa, mutitumize ife tilowe m'gulu la nkhumbazo.


Ndipo panali pamenepo gulu lalikulu la nkhumba zilinkudya kuphiri.


Ndipo panali pamenepo gulu la nkhumba zambiri zilinkudya m'phiri. Ndipo zinampempha Iye kuti azilole zilowe mu izo. Ndipo anazilola.


ndi nkhumba, popeza igawanika chiboda koma yosabzikula, muiyese yodetsa; musamadya nyama yao, musamakhudza mitembo yao.