Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 27:21 - Buku Lopatulika

Koma kazembe anati kwa iwo, Mufuna kuti ndikumasulireni uti wa awa awiri? Ndipo iwo anati, Barabasi.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma kazembe anati kwa iwo, Mufuna kuti ndikumasulireni uti wa awa awiri? Ndipo iwo anati, Barabasi.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Tsono bwanamkubwa uja adaŵafunsa kuti, “Mukufuna kuti ndikumasulireni uti mwa aŵiriŵa?” Anthu aja adati, “Barabasi.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Bwanamkubwayo anafunsa kuti, “Ndi ndani mwa awiriwa amene mufuna ine ndikumasulireni?” Iwo anayankha kuti, “Baraba.”

Onani mutuwo



Mateyu 27:21
6 Mawu Ofanana  

Munandisiyanitsira wodziwana nane kutali; munandiika ndiwakhalire chonyansa. Ananditsekereza, osakhoza kutuluka ine.


Chifukwa chake pamene anasonkhana, Pilato ananena kwa iwo, Mufuna kuti ndikumasulireni yani? Barabasi kodi, kapena Yesu, wotchedwa Khristu?


Koma ansembe aakulu ndi akulu anapangira anthu kuti apemphe Barabasi, koma kuti aononge Yesu.


Pilato ananena kwa iwo, Nanga ndidzachita chiyani ndi Yesu, wotchedwa Khristu? Onse anati, Apachikidwe pamtanda.


Koma olimawo, pamene anamuona, anauzana wina ndi mnzake, nati, Uyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe, kuti cholowa chake chikhale chathu.


Ndipo Pilato anaitana ansembe aakulu, ndi akulu, ndi anthu, asonkhane,