Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 27:12 - Buku Lopatulika

Ndipo pakumnenera Iye ansembe aakulu ndi akulu, Iye sanayankhe kanthu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pakumnenera Iye ansembe aakulu ndi akulu, Iye sanayankhe kanthu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma pamene akulu a ansembe ndi akulu a Ayuda aja ankamuneneza, Yesu sadayankhepo kanthu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Pamene akulu a ansembe ndi akuluakulu ankamuneneza, sanayankhe kanthu.

Onani mutuwo



Mateyu 27:12
10 Mawu Ofanana  

Iye anatsenderezedwa koma anadzichepetsa yekha osatsegula pakamwa pake; ngati nkhosa yotsogoleredwa kukaphedwa, ndi ngati mwanawankhosa amene ali duu pamaso pa omsenga, motero sanatsegule pakamwa pake.


Koma Yesu anangokhala chete. Ndipo mkulu wa ansembe ananena kwa Iye, Ndikulumbiritsa Iwe pa Mulungu wamoyo, kuti utiuze ife ngati Iwe ndiwe Khristu, Mwana wa Mulungu.


Pomwepo Pilato ananena kwa Iye, Sukumva kodi zinthu zambiri zotere akunenera Iwe?


Ndipo sanayankhe Iye, ngakhale mau amodzi, kotero kuti kazembe anazizwa ndithu.


Ndipo anamfunsa Iye mau ambiri; koma Iye sanamyankhe kanthu.


Koma palembo pamene analikuwerengapo ndipo: Ngati nkhosa anatengedwa kukaphedwa, ndi monga mwanawankhosa ali duu pamaso pa womsenga, kotero sanatsegule pakamwa pake.


amene pochitidwa chipongwe sanabwezere chipongwe, pakumva zowawa, sanaopse, koma anapereka mlandu kwa Iye woweruza kolungama;