Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 25:4 - Buku Lopatulika

koma anzeruwo anatenga mafuta m'nsupa zao, pamodzi ndi nyali zao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

koma anzeruwo anatenga mafuta m'nsupa zao, pamodzi ndi nyali zao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma asanu ochenjera aja adaatenga mafuta ena apadera m'nsupa zao.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

koma ochenjerawo anatenga mafuta awo mʼmabotolo pamodzi ndi nyale zawo.

Onani mutuwo



Mateyu 25:4
15 Mawu Ofanana  

Mukonda chilungamo, ndipo mudana nacho choipa, chifukwa chake Mulungu, ndiye Mulungu wanu, wadzoza inu ndi mafuta a chikondwerero koposa anzanu.


Taonani, Ine ndikutumizani inu monga nkhosa pakati pa mimbulu; chifukwa chake khalani ochenjera monga njoka, ndi oona mtima monga nkhunda.


Ndipo asanu a iwo anali opusa, ndi asanu anali ochenjera.


Pakuti opusawo, m'mene anatenga nyali zao, sanadzitengerenso mafuta;


Ndipo pamene mkwati anachedwa, onsewo anaodzera, nagona tulo.


Chifukwa chimenechi yense amene akamva mau anga amenewa, ndi kuwachita, ndidzamfanizira iye ndi munthu wochenjera, amene anamanga nyumba yake pathanthwe;


Pakuti Iye amene Mulungu anamtuma alankhula mau a Mulungu; pakuti sapatsa Mzimu ndi muyeso.


Koma inu simuli m'thupi ai, koma mumzimu, ngatitu Mzimu wa Mulungu akhalabe mwa inu. Koma ngati munthu alibe Mzimu wa Khristu, siali wake wa Khristu.


amenenso anatisindikiza chizindikiro, natipatsa chikole cha Mzimu mu mitima yathu.


Ndipo inu muli nako kudzoza kochokera kwa Woyerayo, ndipo mudziwa zonse.


Ndipo inu, kudzoza kumene munalandira kuchokera kwa Iye, kukhala mwa inu, ndipo simusowa kuti wina akuphunzitseni; koma monga kudzoza kwake kukuphunzitsani za zinthu zonse, ndipo kuli koona, sikuli bodza ai, ndipo monga kudaphunzitsa inu, mukhale mwa Iye.


Iwo ndiwo opatukitsa, anthu a makhalidwe achibadwidwe, osakhala naye Mzimu.