Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 23:11 - Buku Lopatulika

Koma wamkulu wopambana wa inu adzakhala mtumiki wanu.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma wamkulu wopambana wa inu adzakhala mtumiki wanu.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pakati panupa wamkulu akhale mtumiki wanu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Wamkulu pakati panu adzakhala wokutumikirani.

Onani mutuwo



Mateyu 23:11
11 Mawu Ofanana  

Ndipo musatchedwa atsogoleri, pakuti alipo mmodzi Mtsogoleri wanu, ndiye Khristu.


Ndipo m'mene anakhala pansi anaitana khumi ndi awiriwo; nanena nao, Ngati munthu afuna kukhala woyamba, akhale wakuthungo wa onse, ndi mtumiki wa onse.


Pakuti pokhala ndinali mfulu kwa onse, ndinadzilowetsa ndekha ukapolo kwa onse, kuti ndipindule ochuluka.


Kodi ali atumiki a Khristu? (Ndilankhula monga moyaluka), makamaka ine; m'zivutinso mochulukira, m'ndende mochulukira, m'mikwingwirima mosawerengeka, muimfa kawirikawiri.


Pakuti tilalikira si za ife tokha, koma Yesu Khristu Ambuye, ndi ife tokha akapolo anu, chifukwa cha Khristu.


Pakuti adakuitanani inu, abale, mukhale mfulu; chokhacho musachite nao ufulu wanu chothandizira thupi, komatu mwachikondi chitiranani ukapolo.