Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 20:27 - Buku Lopatulika

ndipo aliyense amene akafuna kukhala woyamba mwa inu, adzakhala kapolo wanu:

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

ndipo amene aliyense akafuna kukhala woyamba mwa inu, adzakhala kapolo wanu:

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Ndipo aliyense wofuna kukhala mtsogoleri pakati panu, akhale kapolo wanu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Ndipo aliyense amene akufuna kukhala woyamba akhale kapolo wanu.

Onani mutuwo



Mateyu 20:27
12 Mawu Ofanana  

Chifukwa chake yense amene adzichepetsa yekha monga kamwana aka, yemweyo ali wopambana mu Ufumu wa Kumwamba.


Sikudzakhala chomwecho kwa inu ai; koma aliyense amene akafuna kukhala wamkulu mwa inu, adzakhala mtumiki wanu;


monga Mwana wa Munthu sanadze kutumikiridwa koma kutumikira, ndi kupereka moyo wake dipo la anthu ambiri.


Koma sipadzatero ndi inu; komatu iye ali wamkulu mwa inu, akhale ngati wamng'ono; ndi iye ali woyamba, akhale ngati wotumikira.


Ine ndili wamangawa wa Agriki ndi wa akunja, wa anzeru ndi wa opusa.


Pakuti ndiyesa kuti sindinaperewere konse ndi atumwi oposatu.


Ndipo ndidzapereka ndi kuperekedwa konse chifukwa cha miyoyo yanu mokondweratu. Ngati ndikonda inu kochuluka koposa, kodi ndikondedwa kochepa?


Pakuti tilalikira si za ife tokha, koma Yesu Khristu Ambuye, ndi ife tokha akapolo anu, chifukwa cha Khristu.