Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 15:25 - Buku Lopatulika

Koma iye anadza, namgwadira Iye, nanena, Ambuye, ndithangateni ine.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma iye anadza, namgwadira Iye, nanena, Ambuye, ndithangateni ine.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mai uja adadzamgwadira nati, “Ambuye, ndithu thandizeni.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Mayiyo anabwera ndi kugwada pamaso pake, nati, “Ambuye ndithandizeni!”

Onani mutuwo



Mateyu 15:25
10 Mawu Ofanana  

Ndipo iye anati Ndileke ndimuke, chifukwa kulinkucha. Ndipo Yakobo anati, Sindidzakuleka iwe kuti umuke, ukapanda kundidalitsa ine.


inde, analimbana ndi wamthenga nampambana; analira, nampembedza Iye; anampeza Iye ku Betele, ndi kumeneko Iye analankhula ndi ife;


Ndipo iwo amene anali m'ngalawamo anamgwadira, nanena, Zoonadi, ndinu Mwana wa Mulungu.


Ndipo Iye anayankha, nati, Sichabwino kutenga mkate wa ana, ndi kuuponyera tiagalu.


Ndipo khamulo linawaletsa, kuti atonthole: koma anakuwitsa, nanena, Ambuye, mutichitire chifundo, Inu Mwana wa Davide.


Ndipo onani, wakhate anadza namgwadira Iye, nanena, Ambuye ngati mufuna mungathe kundikonza.


Ndipo kawirikawiri ukamtaya kumoto ndi kumadzi, kumuononga; koma ngati mukhoza kuchita kanthu mtithandize, ndi kutichitira chifundo.


Pomwepo atate wa mwana anafuula, nanena, Ndikhulupirira; thandizani kusakhulupirira kwanga.