Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 14:5 - Buku Lopatulika

Ndipo pofuna kumupha iye, anaopa khamu la anthu, popeza anamuyesa iye mneneri.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Ndipo pofuna kumupha iye, anaopa khamu la anthu, popeza anamuyesa iye mneneri.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kwenikweni Herode ankafuna kupha Yohane, koma ankaopa anthu, chifukwa iwo ankati ndi mneneri.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Herode anafuna kupha Yohane koma iye anaopa anthu chifukwa anamuyesa iye mneneri.

Onani mutuwo



Mateyu 14:5
10 Mawu Ofanana  

ndipo pamene Yehoyakimu mfumu, ndi amphamvu ake onse, ndi akulu onse, anamva mau ake, mfumu inafuna kumupha iye; koma pamene Uriya anamva, anaopa, nathawa, nanka ku Ejipito;


Koma munatulukiranji? Kukaona mneneri kodi? Indetu, ndinena kwa inu, wakuposa mneneri.


Koma tikati, Kwa anthu, tiopa khamulo la anthu; pakuti onse amuyesa Yohane mneneri.


Popeza Yohane anadza kwa inu m'njira ya chilungamo, ndipo simunamvere iye; koma amisonkho ndi akazi achiwerewere anammvera iye; ndipo inu, m'mene munachiona, simunalape pambuyo pake, kuti mumvere iye.


Ndiponso, tikanena, Uchokera kwa anthu; anthu onse adzatiponya miyala: pakuti akopeka mtima, kuti Yohane ali mneneri.


Koma m'mene anawaopsanso anawamasula, osapeza kanthu kakuwalanga, chifukwa cha anthu; pakuti onse analemekeza Mulungu chifukwa cha chomwe chidachitika.


Pamenepo anachoka mdindo pamodzi ndi anyamata; anadza nao, koma osawagwiritsa, pakuti anaopa anthu, angaponyedwe miyala.