Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 14:4 - Buku Lopatulika

Pakuti Yohane ananena kwa iye, Sikuloledwa kwa iwe kukhala naye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Pakuti Yohane ananena kwa iye, Sikuloledwa kwa iwe kukhala naye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Pakuti Yohane adaauza Herode kuti, “Nkulakwira Malamulo kumukwatira mkaziyo.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Chifukwa Yohane anakhala akunena kwa iye kuti, “Sichololedwa kwa inu kutenga mkaziyo.”

Onani mutuwo



Mateyu 14:4
12 Mawu Ofanana  

Ndipo Natani ananena kwa Davide, Munthuyo ndi inu nomwe. Atero Yehova, Mulungu wa Israele, Ndinakudzoza ukhale mfumu ya Israele, ndinakupulumutsa m'dzanja la Saulo;


Ndipo uzilankhula naye, ndi kuti, Atero Yehova, Kodi wapha, nulandanso? Nulankhulenso naye, kuti, Atero Yehova, Paja agalu ananyambita mwazi wa Naboti pompaja agalu adzanyambita mwazi wako, inde wako.


Woipa athawa palibe momthamangitsa; koma olungama alimba mtima ngati mkango.


Omwe asiya chilamulo atama oipa; koma omwe asunga chilamulo akangana nao.


Kuchilamulo ndi kuumboni! Ngati iwo sanena malinga ndi mau awa, ndithu sadzaona mbandakucha.


Ndipo Yeremiya mneneri ananena mau onsewa kwa Zedekiya mfumu ya Yuda mu Yerusalemu,


Usamavula mkazi wa mbale wako; ndiye thupi la mbale wako.


Munthu akatenga mkazi wa mbale wake, chodetsa ichi; wavula mbale wake; adzakhala osaona ana.


Pakuti Yohane adanena kwa Herode, Si kuloledwa kwa inu kukhala naye mkazi wa mbale wanu.