Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Mateyu 14:16 - Buku Lopatulika

Koma Yesu anati kwa iwo, Iwo alibe chifukwa cha kumukira, apatseni ndinu adye.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Koma Yesu anati kwa iwo, Iwo alibe chifukwa cha kumukira, apatseni ndinu adye.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Koma Yesu adaŵauza kuti, “Palibe chifukwa choti achokere. Inuyo apatseni chakudya.”

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Yesu anawayankha kuti, “Sikofunika kuti azipita. Inuyo muwapatse kanthu kuti adye.”

Onani mutuwo



Mateyu 14:16
10 Mawu Ofanana  

Alipo wogawira, nangolemerabe; aliponso womana chomwe ayenera kupatsa nangosauka.


Gawira asanu ndi awiri ngakhale asanu ndi atatu; pakuti sudziwa choipa chanji chidzaoneka pansi pano.


Ndipo pamene panali madzulo, ophunzira ake anafika kwa Iye, nanena, Malo ano nga chipululu, ndipo nthawi yapita tsopano; kauzeni makamuwo amuke, apite kumidzi kukadzigulira okha kamba.


Koma iwo ananena kwa Iye, Ife tilibe kanthu pano koma mikate isanu, ndi nsomba ziwiri.


Koma iye anayankha nanena kwa iwo, Iye amene ali nao malaya awiri apatse kwa iye amene alibe; ndi iye amene ali nazo zakudya achite chomwecho.


Pakuti popeza Yudasi anali nalo thumba, ena analikuyesa kuti Yesu ananena kwa iye, Gula zimene zitisowa pachikondwerero; kapena, kuti apatse kanthu kwa aumphawi.