Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 94:9 - Buku Lopatulika

Kodi Iye wakupanga khutu ngwosamva? Kodi Iye wakuumba diso ngwosapenya?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Kodi Iye wakupanga khutu ngwosamva? Kodi Iye wakuumba diso ngwosapenya?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Kodi amene adalenga makutu, sangathe kumva? Kodi amene adapanga maso, sangathe kupenya?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?

Onani mutuwo



Masalimo 94:9
12 Mawu Ofanana  

Yehova ali mu Kachisi wake woyera, Yehova, mpando wachifumu wake uli mu Mwamba; apenyerera ndi maso ake, ayesa ana a anthu ndi zikope zake.


Mwayesera mtima wanga; mwandizonda usiku; mwandisuntha, simupeza kanthu; mwatsimikiza mtima kuti m'kamwa mwanga simudzalakwa.


Nkhope ya Yehova itsutsana nao akuchita zoipa, kudula chikumbukiro chao padziko lapansi.


Mulungu sakadasanthula ichi kodi? Pakuti adziwa zinsinsi za mtima.


Koma Yehova ananena naye, Anampangira munthu m'kamwa ndani? Kapena analenga munthu wosalankhula ndani, kapena wogontha, kapena wamaso, kapena wakhungu? Si ndine Yehova kodi?


Vinyo achita chiphwete, chakumwa chaukali chisokosa; wosochera nazo alibe nzeru.


Khutu lakumva, ndi diso lopenya, Yehova anapanga onse awiriwo.


Taonani, mkono wa Yehova sufupika, kuti sungathe kupulumutsa; khutu lake silili logontha, kuti silingamve;


Ndipo pakamwa panu mwadzikuza pa Ine, ndi kundichulukitsira mau anu ndawamva Ine.


Ngati thupi lonse likadakhala diso, kukadakhala kuti kununkhiza?