Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 94:8 - Buku Lopatulika

Zindikirani, opulukira inu mwa anthu; ndipo opusa inu, mudzachita mwanzeru liti?

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Zindikirani, opulukira inu mwa anthu; ndipo opusa inu, mudzachita mwanzeru liti?

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Mvetsani anthu opusa kwambirinu. Zitsiru inu, mudzakhala ndi nzeru liti?

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?

Onani mutuwo



Masalimo 94:8
12 Mawu Ofanana  

Pakuti aona anzeru amafa, monga aonongekera wopusa, wodyerera momwemo, nasiyira ena chuma chao.


ndinali wam'thengo, wosadziwa kanthu; ndinali ngati nyama pamaso panu.


Munthu wopulukira sachidziwa; ndi munthu wopusa sachizindikira ichi;


Kodi mudzakonda zazibwana kufikira liti, achibwana inu? Onyoza ndi kukonda kunyoza, opusa ndi kuda nzeru?


Wokonda mwambo akonda kudziwa; koma wakuda chidzudzulo apulukira.


Achibwana inu, chenjerani, opusa inu, khalani ndi mtima wozindikira;


Ponyala nthambi zake zidzathyoledwa; akazi adzafika, nazitentha ndi moto, pakuti ali anthu opanda nzeru; chifukwa chake Iye amene anawalenga sadzawachitira chisoni, ndi Iye amene anawaumba sadzawakomera mtima.


Koma onse pamodzi apulukira ndi kupusa; mtengo ndiwo chilangizo, chopanda pake.


palibe mmodzi wakudziwitsa, palibe mmodzi wakulondola Mulungu;


Akadakhala nazo nzeru, akadazindikira ichi, akadasamalira chitsirizo chao!


Pakuti kale ifenso tinali opusa, osamvera, onyengeka, akuchitira ukapolo zilakolako ndi zokondweretsa za mitundumitundu, okhala m'dumbo ndi njiru, odanidwa, odana wina ndi mnzake.