Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 94:12 - Buku Lopatulika

Wodala munthu amene mumlanga, Yehova; ndi kumphunzitsa m'chilamulo chanu;

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Wodala munthu amene mumlanga, Yehova; ndi kumphunzitsa m'chilamulo chanu;

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Chauta, ngwodala munthu amene mumamlangiza, amene mumamphunzitsa ndi malamulo anu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;

Onani mutuwo



Masalimo 94:12
10 Mawu Ofanana  

Taona, wodala munthu amene Mulungu amdzudzula; chifukwa chake usapeputsa kulanga kwa Wamphamvuyonse.


Ndisanazunzidwe ndinasokera; koma tsopano ndisamalira mau anu.


Kundikomera kuti ndinazunzidwa; kuti ndiphunzire malemba anu.


Mau a Yehova aitana mzinda, ndi wanzeru aopa dzina lanu; tamverani ndodo, ndi Iye amene anaiika.


Koma poweruzidwa, tilangidwa ndi Ambuye, kuti tingatsutsidwe pamodzi ndi dziko lapansi.


Ndipo muzindikire m'mtima mwanu, kuti monga munthu alanga mwana wake, momwemo Yehova Mulungu wanu akulangani inu.


Onse amene ndiwakonda, ndiwadzudzula ndi kuwalanga; potero chita changu, nutembenuke mtima.