Baibulo la pa intaneti

Zotsatsa


Baibulo lonse Chipangano Chakale Chipangano Chatsopano




Masalimo 93:3 - Buku Lopatulika

Mitsinje ikweza, Yehova, mitsinje ikweza mkokomo wao; mitsinje ikweza mafunde ao.

Onani mutuwo

Chichewa Buku Lopatulika Bible 2014

Mitsinje ikweza, Yehova, mitsinje ikweza mkokomo wao; mitsinje ikweza mafunde ao.

Onani mutuwo

Buku Loyera Catholic Edition - Chichewa

Inu Chauta, nyanja zazikulu zakwera, zikukokoma koopsa. Mafunde ake akuchita mkokomo waukulu.

Onani mutuwo

Mawu a Mulungu mu Chichewa Chalero

Nyanja zakweza Inu Yehova, nyanja zakweza mawu ake; nyanja zakweza mafunde ake ochita mkokomo.

Onani mutuwo



Masalimo 93:3
17 Mawu Ofanana  

Zingwe za imfa zinandizinga, ndipo mitsinje ya zopanda pake inandiopsa.


Chinkana madzi ake akokoma, nachita thovu, nagwedezeka mapiri ndi kudzala kwake.


Pali mtsinje, ngalande zake zidzakondweretsa mzinda wa Mulungu. Malo oyera okhalamo Wam'mwambamwamba.


Kumwamba kukondwere nilisekerere dziko lapansi; nyanja ibume mwa kudzala kwake.


Pakuti inu mudzatuluka ndi kukondwa, ndi kutsogozedwa ndi mtendere; mapiri ndi zitunda, zidzaimba zolimba pamaso panu, ndi mitengo yonse ya m'thengo idzaomba m'manja mwao.


Pakuti munandiponya mwakuya m'kati mwa nyanja, ndipo madzi anandizinga; mafunde anu onse a nyondonyondo anandimiza.


Ndipo njokayo inalavula m'kamwa mwake, madzi ngati mtsinje, potsata mkazi, kuti mkaziyo akakokoleredwe nao.


Ndipo anena ndi ine, Madziwo udawaona uko akhalako mkazi wachigololoyo ndiwo anthu, ndi makamu, ndi mitundu, ndi manenedwe.